1. Tamverani mau awa akunenerani Yehova motsutsa, inu ana a Israyeli, kulinenera banja lonse ndinalikweza kuliturutsa m'dziko la Aigupto, ndi kuti,
2. Inu nokha ndinakudziwani mwa mabanja onse a pa dziko lapansi, m'mwemo ndidzakulangani cifukwa ca mphulupulu zanu zonse.
3. Kodi awiri adzayenda pamodzi asanapanganiranetu?