Amosi 1:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo ndidzatyola mpiringidzo wa Damasiko, ndi kulikha okhala m'cigwa ca Aveni, ndi iye wogwira ndodo yacifumu m'Betedeni; ndi anthu a Aramu adzalowa ndende ku Kiri, ati Yehova.

6. Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Gaza, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anatenga ndende anthu onse kuwapereka kwa Edomu;

7. koma ndidzatumiza moto pa linga la Gaza, ndipo udzatha nyumba zace zacifumu;

8. ndipo ndidzalikha okhala m'Asidodi, ndi iye wogwira ndodo yacifumu m'Asikeloni; ndipo ndidzabwezera Ekroni dzanja langa limlange; ndi Afilisti otsala adzatayika, ati Ambuye Yehova.

9. Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Turo, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anapereka anthu onse kwa Edomu, osakumbukila pangano lacibale;

10. koma ndidzatumiza moto pa linga la Turo, ndipo udzanyeketsa nyumba zace zacifumu.

Amosi 1