7. ozika mizu ndi omangirika mwa iye, ndi okhazikika m'cikhulupiriro, monga munaphunzitsidwa, ndi kucurukitsa ciiyamiko.
8. Penyani kuti pasakhale wina wakulanda inu ngati cuma, mwa kukonda nzeru kwace, ndi cinyengo copanda pace, potsata mwambo wa anthu, potsata zoyamba za dziko lapansi, osati potsata Kristu;
9. pakuti mwa iye cikhalira cidzalo ca Umulungu m'thupi,
10. ndipo muli odzazidwa mwa iye, ndiye mutu wa ukulu wonse ndi ulamuliro;