Akolose 2:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakuti ndifuna kuti inu mudziwe nkhawa imene ndiri nayo cifukwa ca inu, ndi iwowa a m'Laodikaya, ndi onse amene sanaone nkhope yanga m'thupi;

2. kuti itonthozeke mitima yao, nalumikizike pamodzi iwo m'cikondi, kufikira cuma conse ca cidzalo ca cidziwitso, kuti akazindikire Iwo cinsinsi ca Mulungu, ndiye Kristu,

3. amene zolemera zonseza nzeru ndi cidziwitso zibisika mwa iye.

Akolose 2