Akolose 1:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. popeza tidamva za cikhulupiriro canu ca mwa Kristu Yesu, ndi cikondi muli naco kwa oyera mtima onse;

5. cifukwa ca ciyembekezo cosungikira kwa inu m'Mwamba, cimene mudacimva kale m'mau a coonadi ca Uthenga Wabwino,

6. umene udafikira kwa inu; monganso m'dziko lonse lapansi umabala zipatso, numakula, monganso mwa inu; kuyambira tsikulo mudamva nimunazindildra cisomo ca Mulungu m'coonadi;

7. monga momwe munaphunzira kwa Epafra kapolo mnzathu wokondedwa, ndiyemtumiki wokhulupirika wa Kristu cifukwa ca ife;

Akolose 1