Akolose 1:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. kuti mukayende koyenera Ambuye kukamkondweretsa monsemo, ndi kubala zipatso mu nchito yonse yabwino, ndi kukula m'cizindikiritso ca Mulungu;

11. olimbikitsidwa m'cilimbiko conse, monga mwa mphamvu ya ulemerero wace, kucitira cipiriro conse ndi kuleza mtima konse pamodzi ndi cimwemwe,

12. ndi kuyamika Atate, amene anatiyeneretsa ife kulandirana nao colowa ca oyera mtima m'kuunika;

13. amene anatilanditsa ife ku ulamuliro wa mdima, natisunthitsa kutilowetsa m'ufumu wa Mwana wa cikondi cace;

14. amene tiri nao maomboledwe mwa iye, m'kukhululukidwa kwa zocimwa zathu;

15. amene ali fanizo la Mulungu wosaonekayo, wobadwa woyamba wa cilengedwe conse;

16. pakuti mwa iye, zinalengedwa zonse za m'mwamba, ndi za padziko, zooneka ndi zosaonekazo, kapena mipando yacifumu, kapena maufumu, kapena maukulu, kapena maulamuliro; zinthu zonse zinalengedwa mwa iye ndi kwa iye.

Akolose 1