Ahebri 9:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Pakuti pamene pali copangiratu pafunika pafike imfa ya wolemberayo.

17. Pakuti copangiratu ciona mphamvu atafa mwini wace; popeza ciribe mphamvu konse pokhala wolemberayo ali ndi moyo;

18. momwemo coyambaconso sicinakonzeka copanda mwazi.

19. Pakuti pamene Mose adalankhulira anthu once lamulo liri lonse monga mwa cilamulo, anatenga mwazi wa ana a ng'ombe ndi mbuzi, pamodzi ndi madzi ndi ubweya wofiira ndi hisope, nawaza buku lomwe, ndi anthu onse,

Ahebri 9