26. Pakuti mkulu wa ansembe wotere anatiyenera ife, woyera mtima, wopanda coipa, wosadetsedwa, wosiyana ndi ocimwa, wakukhala wopitirira miyamba;
27. amene alibe cifukwa ca kupereka nsembe tsiku ndi tsiku monga akulu a ansembe, yoyambira cifukwa ca zoipa za iwo eni, yinayi cifukwa ca zoipa za anthu; pakuti ici anacita kamodzi, kwatha, podzipereka yekha.
28. Pakuti cilamulo cimaika akuru a ansembe anthu, okhala naco cifoko; koma mau a lumbirolo, amene anafika citapita cilamulo, aika Mwana, woyesedwa wopanda cirema ku nthawi zonse.