23. ndi kwa msonkhano wa onse ndi Mpingo wa obadwa oyamba olembedwa m'Mwamba, ndi kwa Mulungu Woweruza wa onse, ndi kwa mizimu ya olungama oyesedwa angwiro,
24. ndi kwa Yesu Nkhoswe ya cipangano catsopano, ndi kwa mwazi wa kuwaza wakulankhula cokoma coposa mwazi wa Abeli.
25. Penyani musakane wolankhulayo. Pakuti ngati iwowa sanapulumuka, pomkana iye amene anawacenjeza padziko, koposatu sitidzapulumuka ife, odzipatulira kwa iye wa Kumwamba;
26. amene mau ace anagwedeza dziko pamenepo; koma tsopano adalonjeza, ndi kuti, Kamodzinso ndidzagwedeza, si dziko lokha, komanso m'mwamba.