Agalatiya 4:23-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Komatu uyo wa mdzakazi anabadwa monga mwa thupi; koma iye wa mfuluyo, anabadwa monga mwa Ionjezano, Izo ndizo zophiphiritsa;

24. pakuti akaziwa ali mapangano awiri, mmodzi wa ku phiri la Sinai, akubalira ukapolo, ndiye Hagara.

25. Koma Hagara ndiye phiri la Sinai, m'Arabiya, nafanana ndi Yerusalemu wa tsopano; pakuti ali muukapolo pamodzi ndi ana ace.

26. Koma, Yerusalemu wa kumwamba uli waufulu, ndiwo amai wathu.

27. Pakuti kwalembedwa,Kondwera, cumba iwe wosabala;Yimba nthungululu, nupfuule iwe wosamva kuwawa kwa kubala;Pakuti ana ace a iye ali mbeta acuruka koposa ana a iye ali naye mwamuna.

28. Koma ife, abale, monga Isake, tiri ana a lonjezano.

29. Komatu monga pompaja iye wobadwa monga mwa thupi anazunza wobadwa monga mwa Mzimu, momwemonso tsopano,

Agalatiya 4