1. Ananu, mverani akukubalani mwa Ambuye, pakuti ici ncabwino.
2. Lemekeza atate wako ndi amako (ndilo lamulo loyamba lokhala nalo lonjezano),
3. kuti kukhale bwino ndi iwe, ndi kuti ukhale wa nthawi yaikuru padziko.
4. Ndipo atate inu, musakwiyitse ana anu; komatu muwalere iwo m'maleredwe ndi cilangizo ca Ambuye.
5. Akapolo inu, mverani iwo amene ali ambuye anu monga mwa thupi, ndi kuwaopa ndi kunthunthumira nao, ndi mtima wanu wosakumbukila kanthu kena, monga kwa Kristu;