7. Pakuti onyenga ambiri adaturuka kulowa m'dziko lapansi, ndiwo amene sabvomereza kuti Yesu Kristu anadza m'thupi, Ameneyo ndiye wonyenga ndi wokana Kristu.
8. Mudzipenyerere nokha, kuti mungataye zimene tazicita, koma kuti mulandire mphotho yokwanira.
9. Yense wakupitirira, wosakhala m'ciphunzitso ca Kristu, alibe Mulungu; iye wakukhala m'ciphunzitso, iyeyo ali nao Arate ndi Mwana.
10. Munthu akadza kwa inu, wosatenga ciphunzitso ici, musamlandire iye kunyumba, ndipo musamlankhule.
11. Pakuti iye wakumlankhula ayanjana nazo nchito zace zoipa.