2 Timoteo 3:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. akukhala nao maonekedwe a cipembedzo, koma mphamvu yace adaikana; kwa iwonso udzipatule,

6. Pakuti mwa iwo akhala akukwawira m'nyumba, nagwira akazi opusa, osenza akatundu a zoipa zao, otengedwa nazo zilakolako za mitundu mitundu:

7. ophunzira nthawi zonse, koma sakhoza konse kufikira ku cizindikiritso ca coonadi.

8. Ndipo monga momwe Yane ndi Yambre anatsutsana naye Mose, kotero iwonso atsutsana naco coonadi; ndiwo anthu obvunditsitsa mtima, osatsimikizidwa pacikhulupiriro.

9. Koma sadzapitirirapo; pakuti kupusa kwao kudzaonekeratu kwa onse, monganso kupusa kwa iwo aja.

10. Koma iwe watsatatsata ciphunzitso canga, mayendedwe, citsimikizo mtima, cikhulupiriro, kuleza mtima, cikondi, cipiriro,

2 Timoteo 3