2 Timoteo 2:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Lingirira cimene ndinena; pakuti Ambuye adzakupatsa cidziwitso m'zonse.

8. Kumbukila Yesu Kristu, wouka kwa akufa, wocokera m'mbeu ya Davide, monga mwa Uthenga Wabwino wanga;

9. m'menemo ndimva zowawa kufikira zomangira, monga wocita zoipa; koma mau a Mulungu samangika.

10. Mwa ici ndipirira zonse, cifukwa ca osankhika, kuti iwonso akapeze cipulumutsoeo ca mwa Kristu Yesu, pamodzi ndi ulemerero wosatha.

2 Timoteo 2