2 Timoteo 2:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. ngati tikhala osakhulupirika, Iyeyu akhala wokhulupirika; pakuti sakhoza kudzikana yekha.

14. Uwakumbutse izi, ndi kuwacitira umboni pamaso pa Ambuye, kuti asacite makani ndi mau osapindulitsa kanthu, koma ogwetsa iwo akumva.

15. Ucite cangu kudzionetsera kwa Mulungu wobvomerezeka, wanchito wopanda cifukwa ca kucita manyazi, wolunjika nao bwino mau a coonadi.

16. Koma pewa nkhani zopanda pace; pakuti adzapitirira kutsata cisapembedzo,

2 Timoteo 2