2 Samueli 2:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo tsikulo nkhondo inakula ndithu. Ndi Abineri ndi anthu a Israyeli anathawa pamaso pa anyamata a Davide.

18. Ndipo analipo ana atatu a Zeruya, ndiwo Yoabu, Abisai ndi Asaheli. Ndipo Asaheli anali waliwiro ngati nyama ya kuthengo.

19. Ndipo Asaheli anapitikitsa Abineri. Ndipo m'kuthamanga kwace sanapambukira kulamanja, kapena kulamanzere, pakutsata Abineri.

20. Pomwepo Abineri anaceuka nati, Kodi ndi iwe Asaheli? iye nayankha, Ndine.

2 Samueli 2