17. Ndipo Abisalomu ananena ndi Husai, Kodi cimeneci ndi cifundo cako ca pa bwenzi lako? unalekeranji kupita ndi bwenzi lako?
18. Husai nanena ndi Abisalomu, lai; koma amene Yehova anasankha ndi anthu awa, ndi anthu onse a Israyeli, ine ndiri wace, ndipo ndidzakhala naye iyeyu.
19. Ndiponso ndidzatumikira yani? si pamaso pa mwana wace nanga? monga ndinatumikira pamaso pa atate wanu, momwemo ndidzakhala pamaso panu,
20. Pomwepo Abisalomu ananena ndi Ahitofeli, Upangire cimene ukuti rikacite.