3. Abisalomu nanena naye, Ona zokamba zako ndizo zabwino ndi zolungama; koma mfumu sinauze wina kuti adzamve za iwe.
4. Abisalomu anatinso, Mwenzi atandiika ine ndikhale woweruza m'dzikomo, kuti munthu yense amene ali ndi mrandu wace kapena cifukwa cace, akadafika kwa ine; ndipo ndikadamcitira zacilungamo!
5. Ndipo kunatero kuti pakusendera munthu ali yense kudzamlambira, iye anatambasula dzanja lace, namgwira, nampsompsona.
6. Abisalomu anacitira zotero Aisrayeli onse akudza kwa mfumu kuti aweruze mrandu wao; comweco Abisalomu anakopa mitima ya anthu a Israyeli.
7. Ndipo kunali pakutha zaka zinai Abisalomu ananena kwa mfumu, Mundilole ndimuke ku Hebroni ndikacite cowinda canga ndinaciwindira Yehova.