25. Ndipo mfumu inanena ndi Zadoki, Ubwererenalo likasa la Mulungu kumudziko; akandikomera mtima Yehova, iye adzandibwezanso, nadzandionetsanso gi, ndi pokhala pace pomwe.
26. Koma iye akatero kuti, Sindikondwera nawe konse; onani, ndine pano, andicitire cimene cimkomera.
27. Ndipo mfumu inanenanso ndi Zadoki wansembeyo, Suli mlauli kodi? ubwere kumudzi mumtendere pamodzi ndi ana ako amuna awiri, Ahimaazi mwana wako ndi Jonatani mwana wa Abyatara.
28. Ona ndidzaima pa madooko a m'cipululu kufikira afika mau ako akunditsimikizira ine.
29. Cifukwa cace Zadoki ndi Abyatara ananyamulanso likasa la Mulungu nafika nalo ku Yerusalemu. Ndipo iwo anakhala kumeneko.