5. Ndipo Jonadabu ananena naye, Ugone pa kama wako ndi kudzikokomeza ulikudwala; ndipo pamene atate wako akadzakuona unene naye, Mulole mlongo wanga Tamara abwere kundipatsa kudya, nakonzere cakudyaco pamaso panga kuti ndicione ndi kucidya ca m'manja mwace.
6. Comweco Amnoni anagona, nadzikokomeza alikudwala; ndipo pamene mfumu inadza kumuona, Amnoni anati kwa mfumuyo, Mulole Tamara mlongo wanga abwere ndi kundipangira timitanda tiwiri pamaso panga, kuti ndikadye ca m'manja mwace.
7. Ndipo Davide anatumiza mau kwao kwa Tamara, kuti, Upite ku nyumba ya mlongo wako Amnoni, numkonzere cakudya,
8. Comweco Tamara anapita ku nyumba ya mlongo wace Amnoni; ndipo iye anali cigonere. Ndipo anatenga ufa naukanda naumba timitanda pamaso pace, nakazinga timitandato.