2 Samueli 11:25-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Pomwepo Davide ananena ndi mthengawo, Udzatero kwa Yoabu, Cisakuipire ici, lupanga limaononga ina ndi mnzace. Onjeza kulimbitsa nkhondo yako pamudzipo, nuupasule; numlimbikitse motere.

26. Ndipo pamene mkazi wa Uriya anamva kuti Uriya mwamuna wace adamwalira, iye analira maliro a mwamuna wace.

27. Ndipo pakuturuka malirowo, Davide anatumiza munthu namtenga afike kwao ku nyumba yace; ndipo iyeyo anakhala mkazi wace nambalira mwana wamwamuna. Koma Yehova anaipidwa ndi cinthu cimene Davide adacita.

2 Samueli 11