25. Pomwepo Davide ananena ndi mthengawo, Udzatero kwa Yoabu, Cisakuipire ici, lupanga limaononga ina ndi mnzace. Onjeza kulimbitsa nkhondo yako pamudzipo, nuupasule; numlimbikitse motere.
26. Ndipo pamene mkazi wa Uriya anamva kuti Uriya mwamuna wace adamwalira, iye analira maliro a mwamuna wace.
27. Ndipo pakuturuka malirowo, Davide anatumiza munthu namtenga afike kwao ku nyumba yace; ndipo iyeyo anakhala mkazi wace nambalira mwana wamwamuna. Koma Yehova anaipidwa ndi cinthu cimene Davide adacita.