1. Ndipo kunali, zitatha zaka makumi awiri m'mene anamanga nyumba ya Yehova, ndi nyumba yace yace,
2. Solomo anamanga midzi imene Huramu adampatsa, nakhalitsamo ana a Israyeli.
3. Ndipo Solomo anamuka ku Hamati Zoba, naugonjetsa.
4. Ndipo anamanga Tadimori m'cipululu, ndi midzi yonse yosungiramo cuma, imene anaimanga m'Hamati.