2 Mbiri 5:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndi mfumu Solomo ndi khamu lonse la Israyeli losonkhana kwa iye anali kulikasa, naphera nsembe, nkhosa ndi ng'ombe zosawerengeka kucuruka kwace.

7. Ndipo ansembe analowa nalo likasa la cipangano la Yehova kumalo kwace m'moneneramo mwa kacisi, m'malo opatulikitsa, pansi pa mapiko a akerubi.

8. Pakuti akerubi anafunyulula mapiko ao pa malo a likasa, ndi akerubi anaphimba likasa ndi mphiko zace pamwamba pace.

9. Ndipo zinatalikitsa mphikozo, kuti nsonga za mphiko zidaoneka kulikasa cakuno ca moneneramo, koma sizinaoneka kubwalo; ndipo ziri komweko mpaka lero lino.

2 Mbiri 5