5. Ndipo muimirire m'malo opatulika, monga mwa magawidwe a nyumba za makolo za abale anu ana a anthu, akhale nalo onse gawo la nyumba ya makolo ya Alevi.
6. Ndipo muphere Paskha, nimudzipatule ndi kukonzera abale anu, kucita monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose.
7. Ndipo Yosiya anapatsa ana a anthu zoweta, ana a nkhosa ndi a mbuzi zikhale zonsezo za nsembe za Paskha kwa ali yense anali komweko; zinafikira zikwi makumi atatu, ndi ng'ombe zikwi zitatu, ndizo zotapa pa cuma ca mfumu.
8. Ndi akulu ace anapatsa nsembe yaufulu kwa anthu, kwa ansembe, ndi kwa Alevi. Hilikiya ndi Zekariya ndi Yehieli, atsogoleri a m'nyumba ya Mulungu, anapatsa ansembe zoweta zazing'ono zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi limodzi, ndi ng'ombe mazana atatu, zikhale nsembe za Paskha.