2 Mbiri 33:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo anacita coipa pamaso pa Yehova, monga umo anacitira Manase atate wace; pakuti Amoni anaphera nsembe mafano osema onse amene adawapanga Manase atate wace, nawatumikira.

23. Koma sanadzicepetsa pamaso pa Yehova, monga umo anadzicepetsera Manase atate wace; koma Amoni amene anacurukitsa kuparamula kwace.

24. Ndipo anyamata ace anampangira ciwembu, namupha m'nyumba yace yace.

25. Koma anthu a m'dziko anapha onse adampangira ciwembu mfumu Amoni; ndi anthu a m'dziko analonga Yosiya mwana wace akhale mfumu m'malo mwace.

2 Mbiri 33