2 Mbiri 27:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yotamu anali wa zaka makumi awiri, mphambu zisanu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka khumi ndi zisanu ndi cimodzi; ndi dzina la mace ndiye Yerusa mwana wa Zadoki.

2. Ndipo anacita zoongoka pamaso pa Yehova, monga umo adacitira atate wace Uziya; pokhapo sanalowa m'Kacisi wa Yehova. Koma anthu anacitabe zobvunda.

3. Anamanga cipata ca kumtunda ca nyumba ya Yehova, ndi pa linga la Ofeli anamanga kwakukuru.

4. Namanga midzi m'mapiri a Yuda, ndi m'nkhalango anamanga nyumba zansanja, ndi nsanja zomwe.

5. Anayambananso ndi mfumu ya ana a Amoni, namgonjetsa, Ndi ana a Amoni anamninkha caka comweci matalente a siliva zana limodzi, ndi miyeso ya tirigu zikwi khumi, ndi ya barele zikwi khumi. Ana a Amoni anabwera nazo zomwezo kwa iye caka caciwiri ndi cacitatu comwe.

2 Mbiri 27