2 Mbiri 24:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pakuti ana a Ataliya mkazi woipa uja anathyola citseko ca nyumba ya Mulungu, natenga zopatulidwa zonse za nyumba ya Yehova kuzipereka kwa Baala.

8. Nilamulira mfumu, ndipo anapanga bokosi, naliika kunja ku cipata ca nyumba ya Yehova.

9. Nalalikira mwa Yuda ndi Yerusalemu, abwere nao kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu anauikira Aisrayeli m'cipululu.

10. Ndipo akalonga onse ndi anthu onse anakondwera, nabwera nazo, naponya m'bokosi mpaka atatha.

11. Ndipo kunali, pamene amabwera nalo bokosi alipenye mfumu, mwa manja a Alevi, nakapenya kuti ndalama zinacurukamo, amadza mlembi wa mfumu, ndi kapitao wa wansembe wamkulu, nakhutula za m'bokosi, nalisenza ndi kubwera nalo kumalo kwace. Anatero tsiku ndi tsiku, nasonkhanitsa ndalama zocuruka.

12. Ndipo mfumu ndi Yehoyada anazipereka kwa iwo akugwira nchito ya utumiki ya nyumba ya Yehova, nalembera amisiri omanga ndi miyala, ndi osema mitengo, akonzenso nyumba ya Yehova; ndiponso akucita ndi citsulo ndi mkuwa alimbitse nyumba ya Yehova.

2 Mbiri 24