2 Mbiri 24:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yoasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi anai; ndi dzina la mace ndiye Zibiya wa ku Beereseba.

2. Ndipo Yoasi anacita zoongoka pamaso pa Yehova masiku onse a Yehoyada wansembe.

3. Ndipo Yehoyada anamtengera akazi awiri, nabala ana amuna ndi akazi.

2 Mbiri 24