2 Mbiri 15:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. koma pamene anatembenukira kwa Yehova Mulungu wa Israyeli m'kusautsidwa kwao, ndi kumfuna, anampeza.

5. Ndipo nthawi zija panalibe mtendere kwa iye wakuturuka, kapena kwa iye wakulowa, koma mabvuto akuru anagwera onse okhala m'maikomo.

6. Ndipo anapasulidwa, mtundu wa anthu kupasula unzace, ndi mudzi kupasula mudzi; pakuti Mulungu anawabvuta ndi masautso ali onse.

7. Koma limbikani inu, manja anu asalende; pakuti ku nchito yanu kuli mphotho.

8. Ndipo pakumva Asa mau awa, ndi cinenero ca Odedi mneneriyo, analimbika mtima, nacotsa zonyansazo m'dziko lonse la Yuda ndi Benjamini, ndi m'midzi adailanda ku mapiri a Efraimu; nakonza guwa la nsembe la Yehova lokhala pakhomo pa likole la Yehova.

9. Namemezaonse a m'Yuda ndi m'Benjamini, ndi iwo akukhala nao ocokera ku Efraimu, ndi Manase, ndi Simeoni; pakuti anamdzera ocuruka ocokera ku Israyeli, pamene anaona kuti Yehova Mulungu wace anali naye.

2 Mbiri 15