2 Mafumu 8:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndi macitidwe ena a Yoramu, ndi zonse anazicita, sizinalembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda.

24. Nagona Yoramu ndi makolo ace, naikidwa pamodzi ndi makolo ace m'mudzi wa Davide; ndipo Ahaziya mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

25. Caka cakhumi ndi ziwiri ca Yoramu mwana wa Ahabu mfumu Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda analowa ufumu wace.

26. Ahaziya ndiye, Wa zaka makumi awiri mphambu ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu caka cimodzi. Ndi dzina la mace ndiye Ataliya mdzukulu wa Omri mfumu ya Israyeli.

2 Mafumu 8