26. Koma Yehova sanakululuka mkwiyo wace waukuru waukali umene adapsa mtima nao pa Yuda, cifukwa ca zoputa zonse Manase adaputa nazo mkwiyo wace.
27. Nati Yehova, Ndidzacotsa Yudanso pamaso panga, monga umo ndinacotsera Israyeli; ndipo ndidzataya mudzi uwu ndidausankha, ndiwo Yerusalemu, ndi nyumba ndidainena, Dzina langa lidzakhala komweko.
28. Macitidwe ena tsono a Yosiya, ndi zonse anazicita, sizilembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?
29. Masiku ace Farao-Neko mfumu ya Aigupto anakwerera mfumu ya Asuri ku mtsinje wa Firate; Ddipo mfumu Yosiya anaturuka kuponyana naye, koma anapha Yosiya ku Megido, atamuona.