8. Ndipo sindidzacotsanso mapazi a Israyeli m'dziko ndidalipereka kwa makolo ao; cokhaci asamalire kucita monga mwa zonse ndawalamulira ndi monga mwa cilamulo conse anawalamulira Mose mtumiki wanga.
9. Koma sanamvera, nawalakwitsa Manase, nawacititsa coipa, kuposa amitundu amene Yehova adawaononga pamaso pa ana a Israyeli.
10. Pamenepo Yehova ananena mwa atumiki ace aneneri, ndi kuti,