2 Akorinto 4:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cifukwa cace popeza tiri nao utumiki umene, monga talandira cifundo, sitifoka;

2. koma takaniza zobisfka za manyazi, osayendayenda mocenjerera, kapena kucita nao mau a Mulungu konyenga; koma ndi maonekedwe a coonadi tidzibvomeretsa tokha ku cikumbu mtima ca anthu onse pamaso pa Mulungu.

3. Koma ngatinso Uthenga Wabwino wathu uphimbika, uphimbika mwa iwo akutayika;

4. mwa amene mulungu wa nthawi yino ya pansi pano unacititsa khungu maganizo ao a osakhulupirira, kuti ciwalitsiro ca Uthenga Wabwino wa ulemerero wa Kristu, amene ali cithunzithunzi ca Mulungu, cisawawalire.

2 Akorinto 4