2 Akorinto 13:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Dziyeseni nokha, ngati muli m'cikhulupiriro, dzitsimikizeni nokha. Kapena simuzindikira kodi za inu nokha kuti Yesu Kristu ali mwa inu? mukapanda kukhala osatsimikizidwa.

6. Koma ndiyembekeza kuti mudzazindikira kuti sitiri osatsimikizidwa.

7. Ndipo tipemphera Mulungu kuti musacite kanthu koipa; sikuti ife tikaoneke obvomerezeka, koma kuti inu mukacite cabwino, tingakhale ife tikhala monga osatsimikizidwa.

8. Pakuti sitikhoza kanthu pokana coonadi, koma pobvomereza coonadi.

9. Pakuti tikondwera, pamene ife tffoka ndi inu muli amphamvu; icinso tipempherera, ndicoungwiro wanu.

10. Cifukwa ca ici ndilembera izi pokhala palibe ine, kuti pokhala ndiri pomwepo ndingacite mowawitsa, monga mwa ulamuliro umene Ambuye anandipatsa ine wakumangirira, ndipo si wakugwetsa.

2 Akorinto 13