1 Yohane 3:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Taonani, cikondico Atate watipatsa, kuti tichedwe ana a Mulungu; ndipo tiri ife otere. Mwa ici dziko lapansi silizindikira ife, popeza silimzindikira iye.

2. Okondedwa, tsopano riri ana a Mulungu, ndipo sicinaoneke cimene tidzakhala. Tidziwa kuti, pa kuoneka iye, tidzakhala ofanana ndi iye, Pakuti tidzamuona iye monga ali.

3. Ndipo yense wakukhala naco ciyembekezo ici pa iye, adziyeretsa yekha, monga Iyeyu ali Woyera.

4. Yense wakucita cimo acitanso kusayeruzika; ndipo cimo ndilo kusayeruzika.

5. Ndipo mudziwa kuti iyeyu anaonekera kudzacotsa macimo; ndipo mwa Iye mulibe cimo.

1 Yohane 3