1 Timoteo 5:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mkulu usamdzudzule, komatu umdandaulire ngati atate; anyamata ngati abale;

2. akazi akulu ngati amai; akazi ang'ono ngati alongo, m'kuyera mtima konse.

3. Citira ulemu amasiye amene ali amasiye ndithu.

4. Koma ngati wamasiye wina ali nao ana kapena adzukulu, ayambe aphunzire iwo kucitira ulemu a m'banja lao, ndi kubwezera akuwabala; pakuti ici ncolandirika pamaso pa Mulungu.

5. Koma iye amene ali wamasiye ndithu, nasiyidwa yekha, ayembekezera Mulungu, nakhalabe m'mapembedzo ndi mapemphero usiku ndi usana.

1 Timoteo 5