1. Ndipo mau a Samueli anafikira kwa Aisrayeli onse. Ndipo Aisrayeli anaturuka kukaponyana nkhondo ndi Afilisti, namanga zithando zao ku Ebenezeri; Afilistiwo namanga m'Afeki.
2. Ndipo Afilistiwo anandandalitsa nkhondo yao pa Aisrayeli; ndipo pokomana nkhondo Aisrayeli anakanthidwa ndi Afilisti. Ndipo anapha kuthengoko anthu zikwi zinai a khamu lao.
3. Ndipo pamene anthu anafika ku zithandozo, akuru a Israyeli anati, Yehova anatikanthiranji lero pamaso pa Afilisti? Tikadzitengere likasa la cipangano la Yehova ku Silo, kuti likabwera pakati pa ife, lidzatipulumutsa m'dzanja la adani athu.