1 Samueli 25:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Samueli anamwalira; ndi Aisrayeli onse anaunjikana pamodzi nalira maliro ace, namuika m'nyumba yace ku Rama. Davide nanyamuka, natsikira ku cipululu ca Parana.

2. Ndipo panali munthu ku Maoni, amene katundu wace anali ku Karimeli; iyeyu anali womveka ndithu, anali nazo nkhosa zikwi zitatu, ndi mbuzi cikwi cimodzi; ndipo analikusenga nkhosa zace ku Karimeli.

3. Tsono dzina la munthuyo ndiye Nabala, ndi dzina la mkazi wace ndiye Abigayeli; ndiye mkazi wa nzeru yabwino, ndi wa nkhope yokongola; koma mwamunayo anali waphunzo ndi woipa macitidwe ace; ndipo iye anali wa banja la Kalebi.

1 Samueli 25