1 Samueli 2:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo ngati munthu akanena naye, Koma adzatentha mafuta tsopano apa, atatha, utenge monga mtima wako ufuna; uyo akanena naye, lai, koma undipatsire iyo tsopanoli, ukapanda kutero ndidzailanda.

17. Ndipo zoipa za anyamatawo zinali zazikuru ndithu pamaso pa Yehova; pakuti anthu anaipidwa ndi nsembe ya Yehova.

18. Koma Samueli anatumikira pamaso pa Yehova akali mwana, atamangira m'cuuno ndi efodi wabafuta.

19. Ndiponso amace akamsokera mwinjiro waung'ono, nabwera nao kwa iye caka ndi caka, pakudza pamodzi ndi mwamuna wace kudzapereka nsembe ya pacaka.

1 Samueli 2