1 Samueli 17:2-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo Sauli ndi anthu a Israyeli anasonkhana, namanga zithando pa cigwa ca Ela, nandandalitsa nkhondo yao kuti akaponyane ndi Afilisti.

3. Ndipo Afilisti anaima paphiri tsidya lija, ndi Aisrayeli anaima paphiri tsidya lina; ndi pakati pao panali cigwa.

4. Ndipo ku zithando za Afilisti kunaturuka ciwinda, dzina lace Goliate wa ku Gati, kutalika kwace ndiko mikono isanu ndi umodzi ndi cikhato.

5. Ndipo anali ndi cisoti camkuwa pamutu pace, nabvala maraya aunyolo, olemera ngati masekeli zikwi zisanu za mkuwa,

1 Samueli 17