5. Ndipo Sauli anafika ku mudzi wa Amaleki, nalalira kucigwa.
6. Ndipo Sauli anauza Akeni kuti, Mukani, cokani mutsike kuturuka pakati pa Aamaleki, kuti ndingakuonongeni pamodzi ndi iwo; pakuti inu munacitira ana a Israyeli onse zabwino, pakufuma iwo ku Aigupto. Comwece Akeni anacoka pakati pa Aamaleki.
7. Ndipo Sauli anakantha Aamaleki, kuyambira pa Havila, dera la ku Suri; ciri pandunji pa Aigupto.
8. Namtenga wamoyo Agagi, mfumu ya Aamaleki, naononga konse konse anthu onse ndi lupanga lakuthwa.