1 Samueli 12:13-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Cifukwa cace siyi mfumu imene munaisankha, imene munandipempha; ndipo taonani, Yehova anakuikirani mfumu.

14. Mukaopa Yehova ndi kumtumikira ndi kumvera mau ace, ndi kusakana lamulo lace la Yehova, ndipo inu ndi mfumu imene iweruza inu mukadzatsata Yehova Mulungu wanu, cabwino.

15. Koma mukapanda kumvera mau a Yehova, ndi kupikisana ndi lamulo la Yehova, dzanja la Yehova lidzatsutsana nanu, monga linatsutsana ndi makolo anu.

1 Samueli 12