1 Mbiri 9:30-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Ndi ana ena a, ansembe anasanganiza cisanganizo ca zonunkhira,

31. Ndi Matitiya wina wa Alevi, ndiye mwana woyamba wa Salumu Mkora, anaikidwa ayang'anire zokazingidwa m'ziwaya.

32. Ndi ena a abale ao, a ana a Akohati, anayang'anira mkate woonekera, kuukonza masabata onse.

33. Ndipo awa ndi oyimba akuru a nyumba za makolo a Alevi, okhala m'zipinda, omasuka ku nchito zina; pakuti anali nayo nchito yao usana ndi usiku.

1 Mbiri 9