30. Ndi ana ena a, ansembe anasanganiza cisanganizo ca zonunkhira,
31. Ndi Matitiya wina wa Alevi, ndiye mwana woyamba wa Salumu Mkora, anaikidwa ayang'anire zokazingidwa m'ziwaya.
32. Ndi ena a abale ao, a ana a Akohati, anayang'anira mkate woonekera, kuukonza masabata onse.
33. Ndipo awa ndi oyimba akuru a nyumba za makolo a Alevi, okhala m'zipinda, omasuka ku nchito zina; pakuti anali nayo nchito yao usana ndi usiku.