1. Ndipo Aisrayeli onse anawerengedwa mwa cibadwidwe cao; ndipo taonani, alembedwa m'buku la mafumu a Israyeli; ndipo Yuda anatengedwa ndende kumka ku Babulo cifukwa ca kulakwa kwao.
2. Okhala m'dziko oyamba tsono, akukhala mwao mwao m'roidzi mwao, ndiwo Israyeli, ansembe, Alevi, ndi Anetini.
3. Ndipo m'Yerusalemu munakhala a ana a Yuda, ndi a ana a Benjamini, ndi a ana a Efraimu ndi Manase: