1 Mbiri 7:27-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Nuni mwana wace, Yoswa mwana wace.

28. Ndipo dziko lao, ndi pokhala pao ndizo Beteli ndi miraga yace, ndi kum'mawa Narani, ndi kumadzulo Gezeri ndi miraga yace, ndi Sekemu ndi miraga yace, mpaka Aza ndi miraga yace;

29. ndi kumalire a ana a Manase; Beteseani ndi miraga yace, Taanaki ndi miraga yace, Megido ndi miraga yace, Dora ndi miraga yace. M'menemo anakhala ana a Yosefe mwana wa Israyeli.

30. Ana a Aseri: Imna, ndi Isva, ndi Isvi, ndi Beriya, ndi Sera mlongo wao.

31. Ndi ana a Beriya: Heberi, ndi Malikieli, ndiye atate wa Birizaiti.

32. Ndi Heberi anabala Yafteti, ndi Someri, ndi Hotamu, ndi Suwa mlongo wao.

33. Ndi ana a Yafteti: Pasaki, ndi Bimali, ndi Asvati. Awa ndi ana a Yafteti.

34. Ndi ana a Semeri: Ahi, ndi Roga, Yehuba, ndi Aramu.

35. Ndi ana a Helemu mbale wace: Zofa, ndi Imna, ndi Selesi, ndi Amali.

36. Ana a Zofa: Suwa, ndi Harineferi, ndi Sauli, ndi Beri, ndi Imra,

37. Bezeri, ndi Hndi, ndi Sama, ndi Silisa, ndi Itirani, ndi Beera.

38. Ndi ana a Yeteri: Yefune, ndi Pisipa, ndi Ara.

39. Ndi ana a Ula: Ara, ndi Hanieli, ndi Rizya.

40. Awa onse ndiwo ana a Aseri, akuru a nyumba za makolo ao, ngwazi zosankhika ndi zamphamvu, akuru mwa akalonga. Oyesedwa mwa cibadwidwe cao otumikira kunkhondo ndiwo amuna zikwi makumi awiri mphambu zisanu ndi cimodzi.

1 Mbiri 7