1 Mbiri 6:47-58 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

47. mwana wa Mali, mwana wa Musi, mwana wa Merari, mwana wa Levi.

48. Ndi abale ao Alevi anaikidwa acite za utumiki ziti zonse za kacisi wa nyumba ya Mulungu.

49. Koma Aroni ndi ana ace adafofukiza pa guwa la nsembe yopsereza, ndi pa guwa la nsembe yofukiza, cifukwa ca nchito yonse ya malo opatulikitsa, ndi kucitira Israyeli cowatetezera, monga mwa zonse Mose mtumiki wa Mulungu adawauza.

50. Ndipo ana a Aroni ndiwo Eleazara mwana wace, Pinehasi mwana wace, Abisua mwana wace,

51. Buki mwana wace, Uzi mwana wace, Zerobiya mwana wace,

52. Merayoti mwana wace, Amariya mwana wace, Ahitubu mwana wace,

53. Zadoki mwana wace, Ahimaazi mwana wace.

54. Pokhala pao tsono monga mwa madera ao m'malire mwao ndi awa: kwa ana a Aroni a mabanja a Akobati, pakuti maere oyamba adagwera iwowa,

55. kwa iwo anapereka Hebroni m'dziko la Yuda, ndi podyetsa pace pozungulira pace;

56. koma minda ya mudzi ndi miraga yace anapatsa Kalebi mwana wa Yefune.

57. Ndi kwa ana a Aroni anapereka midzi yopulumukirako: Hebroni, ndi Libina ndi mabusa ace, ndi Yatiri, ndi Esitemowa ndi mabusa ace,

58. ndi Hileni ndi mabusa ace, ndi Debiri ndi mabusa ace,

1 Mbiri 6