1 Mbiri 5:22-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Pakuti adagwa, nafa ambiri, popeza nkhondoyi nja Mulungu. Ndipo anakhala m'malo mwao mpaka anatengedwa ndende.

23. Ndi ana a limodzi la magawo awiri a pfuko la Manase anakhala m'dziko; anacuruka kuyambira Basana kufikira Baala Herimoni, ndi Seniri, ndi phiri la Herimoni.

24. Ndipo akuru a nyumba za makolo ao ndi awa: Eferi, ndi lsi, ndi Elieli, ndi Azrieli, ndi Yeremiya, ndi Hodaviya, ndi Yadieli, anthu amphamvu ndithu, anthu omveka, akulu a nyumba za makolo ao.

25. Koma analakwira Mulungu wa makolo ao, nacita cigololo, ndi kutsata milungu ya mitundu ya anthu a m'dziko, amene Mulungu adaononga pamaso pao.

26. Ndipo Mulungu wa Israyeli anautsa mzimu wa Puli mfumu ya Asuri, ndi mzimu wa Tigilati Pilesere mfumu ya Asuri, ndiye anawatenga ndende; ndiwo Arubeni, ndi Agadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati, nafika nao ku Hala, ndi Habori, ndi Hara ndi ku mtsinje wa Gozani, mpaka lero lino.

1 Mbiri 5