1 Mbiri 27:28-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. ndi woyang'anira mitengo yaazitona, ndi yamikuyu yokhala kuzidikha kunsi, ndiye Baala Hanani Mgederi; ndi woyang'anira zosungiramo mafuta ndiye Yoasi;

29. ndi woyang'anira ng'ombe zakudya m'Saroni ndiye Sitirai Msaroni; ndi woyang'anira ng'ombe za m'zigwa ndiye Safabi mwana wa Adilai;

30. ndi woyang'anira ngamira ndiye Obili M-israyeli; ndi woyang'anira aburu ndiye Yedeya Mmeronoti;

31. ndi woyang'anira zoweta zazing'ono ndiye Yazizi Mhagiri, Onsewa ndiwo akuru a zolemera zace za Davide.

32. Ndipo Yonatani atate wace wina wa Davide anali phungu, munthu wanzeru ndi mlembi; ndi Yehieli mwana wa Hakimoni anakhala ndi ana a mfumu;

33. ndi Ahitofeli anali phungu wa mfumu, ndi Husai M-ariki anali bwenzi la mfumu;

34. ndi wotsatana ndi Ahitofeli, Yehoyada mwana wa Benaya, ndi Abyatara; koma kazembe wa nkhondo ya mfumu ndiye Yoabu.

1 Mbiri 27