1 Mbiri 23:30-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. ndi kuimirira m'mawa ndi m'mawa kuyamika ndi kulemekeza Yehova, momwemonso madzulo;

31. ndi kupereka nsembe zopsereza zonse kwa Yehova, za masabata, za pokhala mwezi, za nyengo zoikika, kuwerenga kwace monga mwa lemba lace, kosalekeza pamaso pa Yehova;

32. ndi kuti asunge udikiro wa cihema cokomanako, ndi udikiro wa malo opatulika ndi udikiro wa ana a Aroni abale ao, potumikira nyumba ya Yehova.

1 Mbiri 23