25. Pakuti Davide anati, Yehova Mulungu wa Israyeli wapumulitsa anthu ace; ndipo akhala m'Yerusalemu kosatha;
26. ndiponso Alevi asasenzenso kacisi ndi zipangizo zace zonse za utumiki wace.
27. Pakuti monga mwa mau ace otsiriza a Davide, ana a Levi anawerengedwa kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu.
28. Pakuti nchito yao ndiyo kuimirira ana a Aroni, atumikire m'nyumba ya Yehova, m'mabwalo, ndi kuzipinda, ndi kuyeretsa zopatulika zonse; inde nchito za utumiki wa nyumba ya Mulungu;
29. ya mkate woonekera womwe, ndi ya ufa wosalala wa nsembe yaufa, ndi ya timitanda taphanthiphanthi topanda cotupitsa, ndi ya ciwaya, ndi yakukazinga, ndi ya miyeso iri yonse;